Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 22:43-49 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

43. Ndipo anayenda m'njira yonse ya atate wace Asa, osapambukamo; nacita coyenera pamaso pa Yehova, koma misanje sanaicotsa; anthu anapherabe nsembe, nafukiza zonunkhira pamsanje.

44. Ndipo Yehosafati anacitana mtendere ndi mfumu ya Israyeli.

45. Tsono maciddwe ena a Yehosafati, ndi mphamvu anaionetsayo, ndi umo anathira nkhondo, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda?

46. Ndipo anacotsa m'dziko anyamata onyansa aja adatsalira masiku a atate wace Asa.

47. Ndipo m'Edomu munalibe mfumu, koma kazembe wa mfumu.

48. Yehosafati anamanga zombo za ku Tarsisi kukatenga golidi ku Ofiri; koma sizinamuka, popeza zinaphwanyika pa Ezioni Geberi.

49. Pamenepo Ahaziyamwana wa Ahabu ananena ndi Yehosafati, Anyamata anga amuke pamodzi ndi anyamata anu m'zombo. Koma Yehosafati anakana.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 22