Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 22:40-45 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

40. Ndipo Ahabu anagona ndi makolo ace; ndi Ahaziya mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

41. Koma Yehosafati mwana wa Asa anayamba kukhala mfumu ya Yuda caka cacinai ca Ahabu mfumu ya Israyeli.

42. Yehosafati anali wa zaka makumi atatu mphambu zisanu, pamene analowa ufumu, nakhala nifumu zaka makumi awiri mphambu zisanu m'Yerusalemu. Ndi dzina la amace linali Azuba mwana wa Sili.

43. Ndipo anayenda m'njira yonse ya atate wace Asa, osapambukamo; nacita coyenera pamaso pa Yehova, koma misanje sanaicotsa; anthu anapherabe nsembe, nafukiza zonunkhira pamsanje.

44. Ndipo Yehosafati anacitana mtendere ndi mfumu ya Israyeli.

45. Tsono maciddwe ena a Yehosafati, ndi mphamvu anaionetsayo, ndi umo anathira nkhondo, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda?

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 22