Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 21:26-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Ndipo anacita moipitsitsa kutsata mafano, monga mwa zonse amazicita Aamori, amene Yehova adawapitikitsa pamaso pa ana a Israyeli.

27. Ndipo kunali, pakumva Ahabu mau amenewa, anang'amba zobvala zace, nabvala ciguduli pathupi pace, nasala kudya, nagona paciguduli, nayenda nyang'anyang'a.

28. Pamenepo mau a Yehova anadza kwa Eliya wa ku Tisibe, nati,

29. Waona umo wadzicepetsera Ahabu pamaso panga? Popeza adzicepetsa pamaso panga, sindidzafikitsa coipa cimeneci akali moyo iye; koma m'masiku a mwana wace ndidzacifikitsa pa nyumba yace.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 21