Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 20:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Benihadadi mfumu ya Aramu anamemeza khamu lace lonse la nkhondo; ndi mafumu makumi atatu mphambu awiri anali naye, pamodzi ndi akavalo ndi magareta; nakamangira Samaria misasa, naponyana nao nkhondo.

2. Natumiza mithenga lrumudzi kwa Ahabu mfumu ya Israyeli, nati kwa iye,

3. Atero Benihadadi, Siliva wako ndi golidi wako ndi wanga, akazi ako ndi ana ako omwe okometsetsawo ndi anga.

4. Ndipo mfumu ya Israyeli anayankha, nati, Monga mwanena, mbuye wanga mfumu, ndine wanu ndi zonse ndiri nazo.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 20