Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 18:31-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Ndipo Eliya anatenga miyala khumi ndi iwiri, monga mwa ciwerengo ca mafuko a ana a Yakobo, amene mau a Yehova adamfikira, kuti, Dzina lako ndi Israyeli.

32. Ndipo ndi miyalayi anamanga guwa la nsembe m'dzina la Yehova, nazunguniza guwalo ndi mcera, ukulu wace ngati kulandira miyeso iwiri ya mbeu kuzinga guwalo.

33. Ndipo anakonza nkhunizo, naduladula ng'ombe, naiika pankhuni. Nati, Dzazani madzi mbiya zinai, muwathire pa nsembe yopsereza ndi pankhuni.

34. Nati, Bwerezaninso kawiri; nabwerezanso. Nati, Bwerezani katatu; nabwereza katatu.

35. Ndipo madzi anayenda pozinga guwa la nsembe, nadzazanso meerawo ndi madzi.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 18