Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 17:14-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Popeza atero Yehova Mulungu wa Israyeli, Mbiya ya ufa siidzatha, ndipo nsupa ya mafuta siidzacepa, kufikira tsiku lakugwetsa mvula Yehova pa dziko lapansi.

15. Ndipo iye anakacita monga mwa mau a Eliya, nadya iye mwini, ndi iyeyo, ndi a m'nyumba ace, masiku ambiri.

16. Mbiya ya ufa siidatha, ndi nsupa ya mafuta siinacepa, monga mwa mau a Yehova amene ananenetsa Eliya.

17. Ndipo kunali, zitatha izi, mwana wa mkazi mwini nyumbayo anadwala; ndipo pokula nthenda yace, analeka kupuma.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 17