Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 16:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo mau a Yehova akutsutsa Basa anadza kwa Yehu mwana wa Hanani, nati,

2. Popeza ndinakukuza iwe kucokera kupfumbi, ndi kukuika iwe mfumu ya anthu anga Israyeli, koma iwe unayenda m'njira ya Yerobiamu, ndi kucimwitsa anthu anga Israyeli, kuputa mkwiyo wanga ndi macimo ao;

3. taona, ndidzacotsa psiti Basa ndi nyumba yace, ndipo ndidzafanizitsa nyumba yako ndi nyumba ya Yerobiamu mwana wa Nebati,

4. Agaru adzadya ali yense wa Basa amene adzafera m'mudzi, ndipo amene adzafera m'thengo zidzamudya mbalame za m'mlengalenga.

5. Tsono macitidwe ena a Basa, ndi nchito zace, ndi mphamvu zace, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli?

6. Nagona Basa ndi makolo ace, naikidwa ku Tiriza; ndipo Ela mwana wace analowa ufumu m'malo mwace.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 16