Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 13:10-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Tsono iye anayenda njira yina osabwerera njira yomweyo anaidzera pakudza ku Beteli.

11. Ndipo ku Beteli kunakhala mneneri wokalamba, ndipo mwana wace wina anadzamfotokozera macitidwe onse anawacita munthu wa Mulunguyo tsiku lomwelo m'Beteli ndi mau ace anawanena ndi mfumu; inde omwe aja iwo anamfotokozera atate wao.

12. Ndipo atate wao anati kwa iwo, Wapitira njira yiti? popeza ana ace adaona njira analowera munthu wa Mulungu anacokera ku Yudayo.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 13