Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 11:3-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo anali nao akazi mazana asanu ndi awiri, ana akazi a mafumu, ndi akazi acabe mazana atatu; ndipo akazi ace anapambutsa mtima wace.

4. Ndipo kunali, atakalamba Solomo, akazi ace anapambutsa mtima wace atsate milungu yina; ndipo mtima wace sunakhala wangwiro ndi Yehova Mulungu wace monga mtima wa Davide atate wace.

5. Tsono Solomo anatsata Asitoreti fano la anthu a Zidoni, ndi Milikomu fano lonyansitsa la Aamoni.

6. Ndipo Solomo anacita coipa pamaso pa Yehova, osatsata Yehova ndi mtima wonse monga Davide atate wace.

7. Pamenepo Salomo anamangira Kemosi fano lonyansitsa la Amoabu ndi Moleki fano lonyansitsa la ana a Amoni misanje, pa phiri liri patsogolo pa Yerusalemu.

8. Ndipo momwemo anacitiranso akazi ace onse acilendo, amene amafukizira naphera nsembe mafano ao.

9. Ndipo Yehova anakwiya ndi Solomo, pokhala mtima wace unapambuka kwa Yehova Mulungu wa Israyeli, amene adamuonekera kawiri,

10. namlamulira za cinthu comweci, kuti asatsate milungu yina; koma iye sanasunga cimene Yehova anacilamula.

11. Cifukwa cace Yehova ananena ndi Solomo, Popeza cinthu ici cacitika ndi iwe, ndipo sunasunga cipangano canga ndi malemba anga amene ndinakulamulira, zedi, ndidzakung'ambira ufumu ndi kuupatsa mnyamata wako.

12. Koma m'masiku ako sindidzatero cifukwa ca Davide atate wako, koma ndidzaung'ambira m'manja mwa mwana wako;

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 11