Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 1:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. NDIPO mfumu Davide anakalamba nacuruka masiku ace; ndipo iwo anampfunda ndi zopfunda, koma iye sanafundidwa.

2. Pamenepo anyamata ace ananena naye, Amfunire mbuye wanga mfumu namwali, aimirire pamaso pa mfumu namsunge; nagone m'mfukato mwanu, kuti mbuye mfumu yanga afundidwe.

3. Tsono anafunafuna m'malire monse a Israyeli namwali wokongola, napeza Abisagi wa ku-Sunamu, nabwera naye kwa mfumu.

4. Ndipo namwaliyo anali wokongola ndithu, namasunga mfumu namtumikira; koma mfumu sinamdziwa.

5. Pamenepo Adoniya mwana wa Hagiti anadzikuza, nati, Ndikhala mfumu ndine; nadzikonzera agareta ndi apakavalo ndi anthu makumi asanu omtsogolera mothamanga.

6. Ndipo atate wace sadambvuta masiku ace onse, ndi kuti, Wlitero cifukwa ninji? Ndiponso anali munthu wokongola ndithu; napondana ndi Abisalomu.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 1