17. Cifukwa cilamulo cinapatsidwa mwa Mose; cisomo ndicoonadi zinadza mwa Yesu Kristu.
18. Kulibe munthu anaona Mulungu nthawi zonse; Mwana wobadwa yekha wakukhala pa cifuwa ca Atate, Iyeyu anafotokozera.
19. Ndipo umene ndiwo umboni wa Yohane, pamene Ayudaanatuma kwa iye ansembe ndi alembi a ku Yerusalemu akamfunse iye, Ndiwe yani?
20. Ndipo anabvomera, wosakana; nalola kuti, Sindine Kristu.