45. Ndipo 7 anawatsegulira mitima yao, kuti adziwitse malembo;
46. ndipo anati kwa iwo, 8 Kotero kwalembedwa, kuti Kristu amve zowawa, nauke kwa akufa tsiku lacitatu;
47. ndi kuti kulalikidwe m'dzina lace kulapa ndi 9 kukhululukidwa kwa macimo kwa 10 mitundu yonse, kuyambira ku Yerusalemu.
48. 11 Inu ndinu mboni za izi.
49. Ndipo onani, 12 Ine nditumiza pa inu lonjezano la Atate wanga; koma khalani inu m'mudzi muno, kufikira mwabvekedwa ndi mphamvu yocokera Kumwamba.
50. Ndipo anaturuka nao kufikira ku Betaniya; nakweza manja ace, nawadalitsa.
51. Ndipo kunali, 13 pakuwadalitsa iye analekana nao, natengedwa kunka Kumwamba.
52. Ndipo 14 anamlambira iye, nabwera ku Yerusalemu ndi cimwemwe cacikuru;
53. ndipo IS anakhala ci khalire m'Kacisi, nalikuyamika Mulungu, Amen.