18. Tiana, tisakonde ndi mau, kapena ndi lilime, komatu ndi kucita ndi m'coonadi.
19. Umo tidzazindikira kuti tiri ocokera m'coonadi, ndipo tidzakhazikitsa mtima wathu pamaso pace,
20. 1 m'mene monse mtima wathu utitsutsa; cifukwa Mulungu ali wamkuru woposa mitima yathu, nazindikira zonse.
21. Okondedwa, 2 mtima wathu ukapanda kuritsutsa, tiri nako kulimbika mtima mwa Mulungu;
22. ndipo 3 cimene ciri conse tipempha, tilandira kwa iye, cifukwa tisunga malamulo ace, ndipo ticita zomkondweretsa pamaso pace.
23. Ndipo 4 Lamulo lace ndi ili, kuti tikhulupirire dzina la Mwana wace Yesu Kristu, ndi 5 kukondana wina ndi mnzace, monga anatilamulira.
24. Ndipo 6 munthu amene asunga malamulo ace akhala mwa iye, ndi iye mwa munthuyo. Ndipo 7 m'menemo tizindikira kuti akhala mwa ife, kucokera mwa Mzimu amene anatipatsa ife.