9. Momwemonso, akazi adzibveke okha ndi cobvala coyenera, ndi manyazi, ndi cidziletso; osati ndi tsitsi lace loluka, ndi golidi kapena ngale, kapena maraya a mtengo wace wapatali;
10. komatu (umo mokomera akazi akubvomereza kulemekeza Mulungu), mwa nchito zabwino.
11. Mkazi aphunzire akhale wacete m'kumvera konse.
12. Koma sindilola ine kuti mkazi aphunzitse, kapena kulamulira mwamuna; komatu akhale cete.
13. Pakuti Adamu anayamba kulengedwa, pamenepo Heva;
14. ndipo Adamu sananyengedwa, koma mkaziyo ponyengedwa analowa m'kulakwa;
15. koma adzapulumutsidwa mwa kubala mwana, ngati akhala m'cikhulupiriro ndi cikondi ndi ciyeretso pamodzi ndi cidziletso.