29. Ngati si kutero, adzacita ciani iwo amene abatizidwa cifukwa ca akufa? Ngatiakufa saukitsidwa konse, abatizidwa cifukwa ninji cifukwa ca iwo?
30. Nanga 1 ifenso tiri m'moopsya bwanji nthawi zonse?
31. 2 Ndifa tsiku ndi tsiku, ndilumbira pa kudzitamandira kwa inu, abale, kumene ndiri nako mwa Kristu Yesu, Ambuye wathu.
32. 3 Ngati odinalimbana ndi zirombo ku Efeso monga mwa munthu, ndipindulanji? Ngati akufa saukitsidwa, 4 tidye timwepakuti mawa timwalira.
33. Musanyengedwe; 5 mayanjano oipa aipsa makhalidwe okoma
34. 6 Ukani molungama, ndipo musacimwe; pakuti enaalibe cidziwitso ca Mulungu, Ndilankhula kunyaza inu.
35. Koma wina adzati, 7 Akufa aukitsidwa bwanji? Ndipo adza nalorhupi lotani?
36. Wopusa iwe, 8 cimene ucifesa wekha sieikhalitsi'dwanso camoyo, ngati sicifa;
37. ndipo cimene ufesa, sufesa thupi limene lidzakhala, koma mbeu yokhakapenaya tirigu kapena ya, mtundu wina;
38. koma Mulungu iaipatsa thupi mongaafuna; ndi, kwa mbeu yonse thupi lace lace.
39. Nyama yonse siiri imodzimodzi; koma yinandi Ya anthu, ndi yina ndiyo nyama ya zoweta, ndi yina ndiyo nyama ya mbalame, ndi yina ya nsomba.
40. Palinso matupi am'mwamba, ndi matupi apadziko: koma ulemerero wa lam'mwamba ndi wina, ndi ulemerero wa lapadziko ndi winanso.
41. Kuli ulemerero wa dzuwa, ndi ulemerero wina wa mwezi, ndi ulemerero wina wa nyenyezi; pakuti nyenyezi isiyana ndi nyenyezi m'ulemerero.
42. 9 Comweconso kudzakhala kuuka kwa akufa. Lifesedwa m'cibvundi, liukitsidwa m'cisabvundi;