1. Tsegula pa makomo ako Lebano, kuti moto uthe mikungudza yako.
2. Cema, mtengo wamlombwa, pakuti mkungudza wagwa, popeza mitengo yokoma yaipitsidwa; cemani athundu a ku Basani, pakuti nkhalango yocinjirizika yagwa pansi.
3. Mau a kucema kwa abusa! pakuti ulemerero wao waipsidwa; mau a kubangula kwa misona ya mikango! pakuti kudzikuza kwa Yordano kwaipsidwa.
4. Atero Yehova Mulungu wanga: Dyetsani zoweta zakukaphedwa;