15. ndi Kata, ndi Nahalala ndi Simironi, ndi Idala ndi Betelehemu: midzi khumi ndi iwiri ndi miraga yao.
16. Ici ndi colowa ca ana a Zebuloni monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi miraga yao.
17. Maere acinai anamturukira Isakara, kunena za ana a Isakara monga mwa mabanja ao.
18. Ndi malire ao anali ku Yezireeli, ndi Kesulotu, ndi Sunemu;
19. ndi Hafaraimu, ndi Sioni, ndi Anaharati;
20. ndi Rabiti ndi Kisioni, ndi Ebezi;
21. ndi Remeti ndi Eni-ganaimu ndi Eni-hada, ndi Beti-Pazezi;
22. ndi malire anafikira ku Tabori, ndi Sahazuma, ndi Betesemesi; ndi maturukiro a malire ao anali ku Yordano; midzi khumi ndi isanu ndi umodzi ndi miraga yao.
23. Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Isakara, monga mwa mabanja ao, midzi ndi miraga yao.
24. Ndipo maece acisanu analiturukira pfuko la ana a Aseri monga mwa mabanja ao.
25. Ndi malire ao ndiwo Helikati, ndi Hali, ndi Beteni ndi Akisafu;
26. ndi Alameleki, ndi Amadi, ndi Misali; nafikira ku Karimeli kumadzulo ndi ku Sihorilibinati;
27. nazungulira koturukira dzuwa ku Beti-dagoni, nafikira ku Zebuloni ndi ku cigwa ca Ifita-eli, kumpoto ku Beti-emeki, ndi Nehieli; naturukira ku Kabulu kulamanzere,