14. nauzungulira malire kumpoto, kumka ku Hanatoni; ndi maturukiro ace anali ku cigwa ca Ifita-eli;
15. ndi Kata, ndi Nahalala ndi Simironi, ndi Idala ndi Betelehemu: midzi khumi ndi iwiri ndi miraga yao.
16. Ici ndi colowa ca ana a Zebuloni monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi miraga yao.
17. Maere acinai anamturukira Isakara, kunena za ana a Isakara monga mwa mabanja ao.
18. Ndi malire ao anali ku Yezireeli, ndi Kesulotu, ndi Sunemu;
19. ndi Hafaraimu, ndi Sioni, ndi Anaharati;