12. ndi kucokera ku Saridi anazungulira kumka kum'mawa kumaturukira dzuwa, mpaka malire a Kisilotu-tabori; naturuka kumka ku Daberati, nakwera ku Yafia;
13. ndi pocoka pamenepo anapitirira kumka kum'mawa ku Gati-heferi, ku Etikazini; naturuka ku Remoni umene ulembedwa mpaka ku Nea,
14. nauzungulira malire kumpoto, kumka ku Hanatoni; ndi maturukiro ace anali ku cigwa ca Ifita-eli;
15. ndi Kata, ndi Nahalala ndi Simironi, ndi Idala ndi Betelehemu: midzi khumi ndi iwiri ndi miraga yao.
16. Ici ndi colowa ca ana a Zebuloni monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi miraga yao.
17. Maere acinai anamturukira Isakara, kunena za ana a Isakara monga mwa mabanja ao.
18. Ndi malire ao anali ku Yezireeli, ndi Kesulotu, ndi Sunemu;
19. ndi Hafaraimu, ndi Sioni, ndi Anaharati;
20. ndi Rabiti ndi Kisioni, ndi Ebezi;
21. ndi Remeti ndi Eni-ganaimu ndi Eni-hada, ndi Beti-Pazezi;
22. ndi malire anafikira ku Tabori, ndi Sahazuma, ndi Betesemesi; ndi maturukiro a malire ao anali ku Yordano; midzi khumi ndi isanu ndi umodzi ndi miraga yao.