41. Ndipo Yoswa anawakantha kuyambira Kadesi-Barinea mpaka ku Gaza, ndi dziko lonse la Goseni mpaka ku Gibeoni.
42. Ndipo Yoswa anagwira mafwnu awa onse ndi dziko lao nthawi yomweyi; cifukwa Yehova Mulungu wa Israyeli anathirira Israyeli nkhondo.
43. Pamenepo Yoswa ndi Aisrayeli onse naye, anabwerera kucigono ku Giligala.