9. Akacita Iye kulamanzere, sindimpenyerera;Akabisala kulamanja, sindimuona,
10. Koma adziwa njira ndilowayi;Atandiyesa ndidzaturuka ngati golidi.
11. Phazi langa lagwiratu moponda Iye,Ndasunga njira yace, wosapambukamo.
12. Sindinabwerera kusiya malamulo a pa milomo yace;Ndasungitsa mau a pakamwa pace koposa lamulo langa langa.
13. Koma Iye ndiye wa mtima umodzi, adzambweza ndani?Ndi ici cimene moyo wace ucifuna acicita.
14. Pakuti adzacita condiikidwiratu;Ndipo zambiri zotere ziri ndi Iye.