13. Koma Iye ndiye wa mtima umodzi, adzambweza ndani?Ndi ici cimene moyo wace ucifuna acicita.
14. Pakuti adzacita condiikidwiratu;Ndipo zambiri zotere ziri ndi Iye.
15. Cifukwa cace ndiopsedwa pankhope pace;Ndikalingirira, ndicita mantha ndi Iye.
16. Pakuti Mulungu walefula mtima wanga,Ndi Wamphamvuyonse wandiopsa.