9. Koma wolungama asungitsa njira yace,Ndi iye wa manja oyera adzakulabe mumphamvu.
10. Koma bwerani inu nonse, idzani tsono;Pakuti sindipeza mwa inu wanzeru.
11. Masiku anga apitirira, zolingirira zanga zaduka,Zace zace zomwe za mtima wanga.
12. Zisanduliza usiku ukhale usana;Kuunika kuyandikana ndi mdima.
13. Ndikayembekezera kumanda kukhale nyumba yanga;Ndikayala pogona panga mumdima.
14. Ndikati kwa dzenje, Ndiwe atate wanga;Kwa mphutsi, Ndiwe mai wanga ndi mlongo wanga;
15. Ciri kuti ciyembekezo canga?Inde, ciyembekezo canga adzaciona ndani?
16. Cidzatsikira ku mipingiridzo ya kumanda,Pamene tipumulira pamodzi kupfumbi.