20. Ana ako amuna akomoka; agona pamtu pa makwalala onse, monga nswala muukonde; adzala ndi ukali wa Yehova, kudzudzula kwa Mulungu wako,
21. Cifukwa cace imva ici tsopano, iwe wobvutidwa ndi woledzera koma si ndi vinyo ai;
22. atero Ambuye ako Yehova, ndi Mulungu wako amene anena mlandu wa anthu ace, Taona, ndacotsa m'dzanja mwako cikho conjenjemeretsa, ngakhale mbale ya cikho ca ukali wanga; iwe sudzamwa ico kawirinso.
23. Ndidzaciika m'dzanja la iwo amene abvutitsa iwe; amene anena ku moyo wako, Gwada pansi kuti ife tipite; ndipo iwe wagonetsa pamsana pako monga pansi, ndi monga khwalala kwa iwo amene apita pamenepo.