13. Watopa mu uphungu wako wambiri; aimirire tsopano openda zam'mwamba, oyang'ana nyenyezi, akuneneratu mwezi ndi mwezi, ndi kukupulumutsa pa zinthu zimene zidzakugwera.
14. Taona, iwo adzakhala ngati ziputu, moto udzawatentha iwo; sadzadzipulumutsa okha ku mphamvu za malawi; motowo sudzakhala khala loothako, pena moto wakukhalako.
15. Zinthu zomwe unagwira nchito yace, zidzatero nawe; iwo amene anacita malonda ndi iwe ciyambire pa ubwana wako, adzayenda yense kunka kumalo kwace; sipadzakhala wopulumutsa iwe.