13. Mitundu ya anthu idzathamanga ngati kuthamanga kwa madzi ambirimbiri; koma Iye adzawadzudzula, ndipo iwo adzathawira patari, nadzapitikitsidwa monga mankhusu a pamapiri patsogolo pa mphepo, ndi monga pfumbi lokwetera patsogolo pa mkunthu wa mphepo.
14. Pa nthawi ya madzulo, taonani kuopsya; kusanace, iwo palibe. Ili ndi gawo la iwo amene atifunkha ndi ici ciwagwera omwe alanda zathu.