1. Ndipo padzaturuka mphukira pa tsinde la Jese, ndi nthambi yoturuka m'mizu yace idzabala zipatso;
2. ndipo mzimu wa Yehova udzambalira iye mzimu wanzeru ndi wakuzindikira, mzimu wa uphungu ndi mphamvu, mzimu wakudziwa ndi wakuopa Yehova;
3. ndipo adzakondwera nako kumuopa Yehova, ndipo sadzaweruza monga apenya maso, sadzadzudzula mwamphekesera: