1. Ananu a Benjamini, pulumukani pothawa pakati pa Yerusalemu, ombani lipenga m'Tekoa, kwezani cizindikiro m'Beti-hakeremu; pakuti caoneka coipa coturuka m'mpoto ndi kuononga kwakukulu.
2. Ndidzacotsa mwana wamkazi wa Ziyoni mkazi wokoma ndi wololopoka.