31. Ndipo panali caka ca makumi atatu ndi zisanu ndi ziwiri ca undende wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda, mwezi wakhumi ndi iwiri, tsiku la makumi awiri ndi asanu la mwezi, Evili-Merodaki mfumu ya ku Babulo anaweramutsa mutu wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda, namturutsa iye m'ndende;
32. nanena naye bwino, naika mpando wace upose mipando ya mafumu amene anali naye m'Babulo.
33. Ndipo anapindula zobvala zace za m'ndende, ndipo sanaleka kudya pamaso pace masiku onse a moyo wace.
34. Koma phoso lace mfumu ya ku Babulo sanaleka kumpatsa, phoso tsiku ndi tsiku gawo lace, mpaka tsiku la kufa kwace, masiku onse a moyo wace.