40. Monga muja Yehova anagwetsa Sodomu ndi Gomora ndi midzi Inzace, ati Yehova; anthu sadzakhalamo, mwana wa munthu sadzagonamo.
41. Taonani, anthu acokera kumpoto; ndiwo mtundu waukuru, ndipo mafumu ambiri adzaukitsidwa kucokera ku malekezero a dziko lapansi.
42. Agwira uta ndi nthungo; ali ankharwe, alibe cifundo; mau ao apokosera ngati nyanja, ndipo akwera akavalo, yense aguba monga munthu wa kunkhondo, kukamenyana ndi iwe, mwana wamkazi wa Babulo.