1. Ndipo Zedekiya mwana wa Yosiya anakhala mfumu m'malo a Koniya mwana wa Yehoyakimu, amene Nebukadirezara mfumu ya ku Babulo inamlowetsa mfumu m'dziko la Yuda.
2. Koma ngakhale iye, ngakhale atumiki ace, ngakhale anthu a padziko, sanamvere mau a Yehova, amene ananena mwa Yeremiya mneneri.