2. Yehova atero kwa ine: Udzipangire zomangira ndi magori, nuziike pakhosi pako;
3. nuzitumize kwa mfumu ya Edomu, ndi kwa mfumu ya Moabu, ndi kwa mfumu ya ana a Amoni, ndi kwa mfumu ya Turo, ndi kwa mfumu ya Zidoni, ndi dzanja la amithenga amene afika ku Yerusalemu kwa Zedekiya mfumu ya Yuda;
4. nuwauze iwo anene kwa ambuyao, kuti, Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli atero: Muzitero kwa ambuyanu: