4. Ndipo mapangidwe ace a coikapo nyali ndiwo golidi wosula; kuyambira tsinde lace kufikira maluwa ace anacisula; monga mwa maonekedwe ace Yehova anaonetsa Mose, momwemo anacipanga coikapo nyali.
5. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
6. Uwatenge Alevi pakati pa ana a Israyeli, nuwayeretse.
7. Ndipo utere nao kuwayeretsa: uwawaze madzi akucotsa zoipa, ndipo apititse lumo pa thupi lao lonse, natsuke zobvala zao, nadziyeretse.
8. Pamenepo atenge ng'ombe yamphongo ndi nsembe yace yaufa, ufa wosanganiza ndi mafuta; utengenso ng'ombe yamphongo yina ikhale nsembe yaucimo.
9. Ndipo ubwere nao Alevi pakhomo pa cihema cokomanako; nuwasonkhanitse khamu lonse la ana a Israyeli;
10. nubwere nao Alevi pamaso pa Yehova; ndi ana a Israyeli aike manja ao pa Alevi;