28. Koma ngati mkazi sanadetsedwa, nakhala woyera, pamenepo adzapulumuka, nadzaima.
29. Ici ndi cilamulo ca nsanje, pamene mkazi, pokhala naye mwamuna wace, ampatukira nadetsedwa;
30. kapena pamene mtima wansanje umgwira mwamuna, ndipo acitira mkazi wace nsanje; pamenepo aziika mkazi pamaso pa Yehova, ndipo wansembe amcitire cilamulo ici conse.
31. Mwamunayo ndiye wosacita mphulupulu, koma mkazi uyo asenze mphulupulu yace.