1. Ndipo mwezi wacisanu ndi ciwiri, tsiku loyamba la mweziwo, muzikhala nako kusonkhana kopatulika; musamacita nchito ya masiku ena; likukhalireni inu tsiku lakuliza malipenga.
2. Pamenepo muzipereka nsembeyopsereza ya pfungo lokoma kwa Yehova; ng'ombe imodzi yamphongo, nkhosa yamphongo imodzi, ana a nkhosa asanu ndi awiri a caka cimodzi opanda cirema;