25. Usaope zoopsya zodzidzimutsa,Ngakhale zikadza zopasula oipa;
26. Pakuti Yehova adzalimbitsa mtima wako,Nadzasunga phazi lako lingakodwe.
27. Oyenera kulandira zabwino usawamane;Pokhoza dzanja lako kuwacitira zabwino.
28. Usanene kwa mnzako, Ukabwerenso,Ndipo mawa ndidzakupatsa;Pokhala uli nako kanthu.
29. Usapangire mnzako ciwembu;Popeza akhala nawe pafupi osatekeseka.
30. Usakangane ndi munthu cabe,Ngati sanakucitira coipa,
31. Usacitire nsanje munthu waciwawa;Usasankhe njira yace iri yonse.
32. Pakuti wamphulupulu anyansa Yehova;Koma cinsinsi cace ciri ndi oongoka.
33. Mulungu atemberera za m'nyumba ya woipa;Koma adalitsa mokhalamo olungama.
34. Anyozadi akunyoza,Koma apatsa akufatsa cisomo.
35. Anzeru adzalandira ulemu colowa cao;Koma opusa adzakweza manyazi.