18. Ndiyo mtengo wa moyo wa akuigwira;Wakulumirira ngwodala.
19. Yehova anakhazika dziko ndi nzeru;Naika zamwamba ndi luntha.
20. Zakuya zinang'ambika ndi kudziwakwace;Thambo ligwetsa mame.
21. Mwananga, zisacokere ku maso ako;Sunga nzeru yeniyeni ndi kulingalira;
22. Ndipo mtima wako udzatengapo moyo,Ndi khosi lako cisomo.
23. Pompo udzayenda m'njira yako osaopa,Osapunthwa phazi lako.
24. Ukagona, sudzacita mantha;Udzagona tulo tokondweretsa.
25. Usaope zoopsya zodzidzimutsa,Ngakhale zikadza zopasula oipa;