8. Wolingalira zakucita zoipaAnthu adzamcha waciwembu.
9. Maganizo opusa ndiwo cimo;Wonyoza anyansa anthu.
10. Ukalefuka tsiku la tsokaMphamvu yako icepa.
11. Omwe atengedwa kuti akafe, uwapulumutse;Omwe ati aphedwe, usaleke kuwalanditsa.
12. Ukanena, Taonani, sitinadziwa cimeneci;Kodi woyesa mitima sacizindikira ici?Ndi wosunga moyo wako kodi sacidziwa?Ndipo kodi sabwezera munthu yense monga mwa macitidwe ace?
13. Mwananga, idya uci pakuti ngwabwino,Ndi cisa cace citsekemera m'kamwamwako;
14. Potero udzadziwa kuti nzeru iri yotero m'moyo wako;Ngati waipeza padzakhala mphotho,Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.
15. Usabisalire, woipa iwe, pomanga wolungama;Usapasule popuma iyepo.
16. Pakuti wolungama amagwa kasanu ndi kawiri, nanyamukanso;Koma oipa akhumudwa pomfikira tsoka.
17. Usakondwere pakugwa mdani wako;Mtima wako usasekere pokhumudwa iye;
18. Kuti Yehova angaone kukondwa kwako, ndi kukuyesa koipa,Ndi kuleka kumkwiyira.
19. Usabvutike mtima cifukwa ca ocita zoipa;Ngakhale kucitira nsanje amphulupulu;