21. Wosowa nzeru akondwera ndi utsiru;Koma munthu wozindikira aongola mayendedwe ace.
22. Zolingalira zizimidwa popanda upoKoma pocuruka aphungu zikhazikika.
23. Munthu akondwera ndi mayankhidwe a m'kamwa mwace;Ndi mau a pa nthawi yace kodi sali abwino?
24. Anzeru ayesa njira yamoyo yokwerakwera,Kuti apambuke kusiya kunsi kwa manda.
25. Yehova adzapasula nyumba ya wonyada;Koma adzalembera mkazi wamasiye malire ace,