11. Cuma colandiridwa mokangaza cidzacepa;Koma wokundika ndi dzanja adzaona zocuruka.
12. Ciyembekezo cozengereza cidwalitsa mtima;Koma pakufika cifuniroco ndico mtengo wa moyo.
13. Wonyoza mau adziononga yekha;Koma woopa malangizo adzalandira mphotho.
14. Malamulo a wanzeru ndiwo kasupe wa moyo,Apatutsa ku misampha ya imfa.
15. Nzeru yabwino ipatsa cisomo;Koma njira ya aciwembu iri makolokoto.
16. Yense wocenjera amacita mwanzeru:Koma wopusa aonetsa utsiru.
17. Mthenga wolakwa umagwa m'zoipa;Koma mtumiki wokhulupirika alamitsa.
18. Wokana mwambo adzasauka nanyozedwa;Koma wolabadira cidzudzulo adzalemekezedwa.
19. Cifuniro cikondweretsa moyo citacitidwa;Koma kusiya zoipa kunyansa opusa,
20. Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru:Koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.
21. Zoipa zilondola ocimwa;Koma olungama adzalandira mphotho yabwino.
22. Wabwino asiyira zidzukulu zace colowa cabwino;Koma wocimwa angosungira wolungama cuma cace.
23. M'kulima kwa osauka muli zakudya zambiri;Koma zinazo zimaonongeka posowa ciweruzo.
24. Wolekereramwanace osammenya amuda;Koma womkonda amyambize kumlanga.
25. Wolungama adya nakhutitsa moyo wace;Koma mimba ya oipa idzasowa.