9. Pakuti izi ndi korona wa cisomo pamtu pako,Ndi mkanda pakhosi pako.
10. Mwananga, akakukopa ocimwa usalole.
11. Akanena, Idza nafe, tibisalire mwazi,Tilalire osacimwa opanda cifukwa;
12. Tiwameze ali ndi moyo ngati manda,Ali amphumphu, ngati akutsikira kudzenje;
13. Tidzapeza cuma conse ca mtengo wace,Tidzadzaza nyumba zathu ndi zofunkha;
14. Udzacita nafe maere,Tonse tidzakhala ndi cibeti cimodzi;
15. Mwananga, usayende nao m'njira;Letsa phazi lako ku mayendedwe ao;
16. Pakuti mapazi ao athamangira zoipa,Afulumira kukhetsa mwazi.