10. Kodi Iye wakulangiza mitundu ya anthu, ndiye wosadzudzula?Si ndiye amene aphunzitsa munthu nzeru?
11. Yehova adziwa zolingalira za munthu,Kuti ziri zacabe.
12. Wodala munthu amene mumlanga, Yehova;Ndi kumphunzitsa m'cilamulo canu;
13. Kuti mumpumitse masiku oipa;Kufikira atakumbira woipa mbuna.
14. Pakuti Yehova sadzasiya anthu ace,Ndipo sadzataya colandira cace.
15. Pakuti ciweruzo cidzabwera kumka kucilungamo:Ndipo oongoka mtima onse adzacitsata.
16. Adzandiukira ndani kutsutsana nao ocita zoipa?Adzandilimbikira ndani kutsutsana nao ocita zopanda pace?