7. Pambali pako padzagwa cikwi,Ndi zikwi khumi pa dzanja lamanja lako;Sicidzakuyandikiza iwe.
8. Koma udzapenya ndi maso ako,Nudzaona kubwezera cilango oipa.
9. Popeza udati, Inu Yehova, ndinu pothawirapo pangaUdaika Wam'mwambamwamba cokhalamo cako;
10. Palibe coipa cidzakugwera,Ndipo colanga sicidzayandikiza hema wako.