12. Adzakunyamula pa manja ao,Ungagunde phazi lako pamwala.
13. Udzaponda mkango ndi mphiri;Udzapondereza msona wa mkango ndi cinjoka:
14. Popeza andikondadi ndidzampulumutsa;Ndidzamkweza m'mwamba, papeza adziwa dzina langa.
15. Adzandipfuulira Ine ndipo ndidzamyankha;Kunsautso ndidzakhala naye pamodzi;Ndidzamlanditsa, ndi kumcitira ulemu.
16. Ndidzamkhutitsa ndi masiku ambiri,Ndi kumuonetsera cipulumutso canga,