1. Ambuye, Inu munatikhalira mokhalamoM'mibadwo mibadwo.
2. Asanabadwe mapiri,Kapena musanalenge dziko lapansi, ndi lokhalamo anthu,Inde, kuyambira nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha,Inu ndinu Mulungu.
3. Mubweza munthu akhale pfumbi;Nimuti, Bwererani inu, ana a anthu.