7. Masiku ace wolungama adzakhazikika;Ndi mtendere wocuruka, kufikira sipadzakhala mwezi.
8. Ndipo adzacita ufumu kucokera kunyanja kufikira kunyanja,Ndi kucokera ku Mtsinje kufikira malekezero a dziko lapansi.
9. Okhala m'cipululu adzagwadira pamaso pace;Ndi adani ace adzaluma nthaka.
10. Mafumu a ku Tarisi ndi ku Zisumbuzo adzabwera naco copereka;Mafumu a ku Sheba ndi Seba adzadza nazo mphatso,
11. Inde mafumu onse adzamgwadira iye:Amitundu onse adzamtumikira.
12. Pakuti adzapulumutsa waumphawi wopfuulayo;Ndi wozunzika amene alibe mthandizi.
13. Adzacitira nsoni wosauka ndi waumphawi,Nadzapulumutsa moyo wa aumphawi,
14. Adzaombola moyo wao ku cinyengo ndi ciwawa;Ndipo mwazi wao udzakhala wa mtengo pamaso pace:
15. Ndipo iye adzakhala ndi moyo; ndipo adzampatsa golidi wa ku Sheba;Nadzampempherera kosalekeza;Adzamlemekeza tsiku lonse.
16. M'dzikomo mudzakhala dzinthu dzocuruka pamwamba pa mapiri;Zipatso zace zidzati waa, ngati za ku Lebano:Ndipo iwo a m'mudzi adzaphuka ngati msipu wapansi.
17. Dzina lace lidzakhala kosatha:Momwe likhalira dzuwa dzina lace lidzamvekera zidzukulu:Ndipo anthu adzadalitsidwa mwa Iye;Amitundu onse adzamucha wodala.
18. Wolemekezeka Yehova Mulungu, Mulungu wa Israyeli,Amene acita zodabwiza yekhayo:
19. Ndipo dzina lace la ulemerero lidalitsike kosatha;Ndipo dziko lonse lapansi lidzale nao ulemerero wace.Amen, ndi Amen.
20. Mapemphero a Davide mwana wa Jese atha.