3. Mapiri adzatengera anthu mtendere,Timapiri tomwe, m'cilungamo.
4. Adzaweruza ozunzika a mwa anthu,Adzapulumutsa ana aumphawi,Nadzaphwanya wosautsa.
5. Adzakuopani momwe likhalira dzuwa ndi mwezi,Kufikira mibadwo mibadwo.
6. Adzanga mvula yakugwa pa udzu wosenga:Monga mvula yothirira dziko.
7. Masiku ace wolungama adzakhazikika;Ndi mtendere wocuruka, kufikira sipadzakhala mwezi.