1. Patsani mfumu maweruzo anu, Mulungu,Ndi mwana wa mfumu cilungamo canu.
2. Potero adzanenera anthu anu mlandu ndi m'cilungamo,Ndi ozunzika anu ndi m'ciweruzo.
3. Mapiri adzatengera anthu mtendere,Timapiri tomwe, m'cilungamo.
4. Adzaweruza ozunzika a mwa anthu,Adzapulumutsa ana aumphawi,Nadzaphwanya wosautsa.