3. Mundikhalire thanthwe lokhalamo, lopitako kosaleka;Mwalamulira kundipulumutsa;Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa,
4. Ndilanditseni, Mulungu wanga, m'dzanja la woipa,M'dzanja la munthu wosalungama ndi waciwawa.
5. Pakuti Inu ndinu ciyembekezo canga, Ambuye Yehova;Mwandikhalira wokhulupirika kuyambira ubwana wanga.
6. Inu munandigwirizizakuyambira ndisanabadwe:Kuyambira pa thupi la mai wanga wondicitira zokoma ndinu;Ndidzakulemekezani kosalekeza.
7. Ndikhala codabwiza kwa ambiri;Koma Inu ndinu pothawira panga polimba.
8. M'kamwa mwanga mudzadzala lemekezo lanu,Ndi ulemu wanu tsiku lonse.
9. Musanditaye mu ukalamba wanga;Musandisiye, pakutha mphamvu yanga.
10. Pakuti adani anga alankhula za ine;Ndipo iwo akulalira moyo wanga apangana upo,
11. Ndi kuti, Wamsiya Mulungu:Mlondoleni, mgwireni; popeza palibe wompulumutsa,
12. Musandikhalire kutali, Mulungu;Fulumirani kundithandiza, Mulungu;
13. Adani a moyo wanga acite manyazi, nathawe;Cotonza ndi cimpepulo zikute ondifunira coipa,
14. Koma ine ndidzayembekeza kosaleka,Ndipo ndidzaonjeza kukulemekezani.
15. Pakamwa panga padzafotokozera cilungamo canu,Ndi cipulumutso canu tsiku lonse;Pakuti sindidziwa mawerengedwe ace.
16. Ndidzamuka mu mphamvu ya Ambuye Yehova;Ndidzachula cilungamo canu, inde canu cokha.
17. Mulungu, mwandiphunzitsa kuyambira ubwana wanga;Ndipo kufikira lero ndilalikira zodabwiza zanu.