12. Musandikhalire kutali, Mulungu;Fulumirani kundithandiza, Mulungu;
13. Adani a moyo wanga acite manyazi, nathawe;Cotonza ndi cimpepulo zikute ondifunira coipa,
14. Koma ine ndidzayembekeza kosaleka,Ndipo ndidzaonjeza kukulemekezani.
15. Pakamwa panga padzafotokozera cilungamo canu,Ndi cipulumutso canu tsiku lonse;Pakuti sindidziwa mawerengedwe ace.
16. Ndidzamuka mu mphamvu ya Ambuye Yehova;Ndidzachula cilungamo canu, inde canu cokha.
17. Mulungu, mwandiphunzitsa kuyambira ubwana wanga;Ndipo kufikira lero ndilalikira zodabwiza zanu.
18. Poteronso pokalamba ine ndi kukhala nazo imvi musandisiye, Mulungu;Kufikira nditalalikira mbadwo uwu za dzanja lanu,Mphamvu yanu kwa onse akudza m'mbuyo.
19. Cilungamo canunso, Mulungu, cifikira kuthambo;Inu amene munacita zazikuru,Akunga Inu ndani, Mulungu?
20. Inu, amene munationetsa nsautso zambiri ndi zoipa,Mudzatipatsanso moyo,Ndi kutitenganso munsi mwa dziko.
21. Mundionjezere ukulu wanga,Ndipo munditembenukire kundisangalatsa,